Malawi News

Atupele Muluzi ndi DPP ubale wawora, polavula moto kuti Mutharika wakalamba

Ubale wa chipani cha Democratic Progressive (DPP) ndi United Democratic Front (UDF) watekeseka ndipo atsirana mphepo pomwe mtsogoleri wa chipani cha UDF Atupele Muluzi watsindika kuti a Peter Mutharika akula ndipo akuyenera akapume.


A Muluzi anayankhula mawuwa pa msonkhano m’boma la Machinga, pomwe ati dziko la Malawi silikuyenera kubweleranso m’mbuyo, ndipo kuti a Mutharika akula akuyenera akapume.


Wonderful Mkhutche
Mkhutche: A Muluzi aonetsa makaka awo.

“A Malawi sitikuyenera kubweleranso m’mbuyo, ine a Mutharika ndimawalemekeza koma akula akapume, nthawi ino ndi ya achinyamata,” anatelo Atupele Muluzi.


Mawuwa sanakondweletse chipani cha DPP chomwe oyankhulira chipanichi Shadrec Namalomba wati mawu omwe ayankhula a Muluzi ndi amtopola ndipo amangoyenera kuti apite ku misonkhano kukadzigulitsa okha osati kumakamba za nyumba ya DPP.


A Namalomba ati anthu anasiya kuwakhulupilira a Muluzi chifukwa ndi munthu yemwe sadziwa ndale ndipo amangowoneka mu nthawi ya chisankho chokha basi.


“Kodi a muluziwo ndi ndani kuti akayankhule za DPP, ndi ndani iwowo?” Anatelo a Namalomba m’chizungu.


Pa masankho a m’chaka cha 2020, a Peter Mutharika adasankha Atupele Muluzi kukhala yemwe ayende naye kupita ku masankho mu mgwirizano omwe awiriwa anagwamo koma sunaphule kanthu pomwe anagwa pamaso pa mgwirizano wa zipani 9 wa Tonse.


M’modzi mwa olankhulapo pa zochitika yemwenso ndi katswiri pa ndale Wonderful Mkhutche wati zikuwonetseratu makaka amene akuwonetsa a Muluzi akukonza njira yofuna kupanga m’gwirizano ndi a Lazarus Chakwera a chipani cha Malawi Congress (MCP).


A Peter Mutharika, Atupele Muluzi ndi a Lazarus Chakwera onse akatenga zikalata ku bungwe la MEC zofuna kupikisana nawo mu masankho a mu September.