Malawi News

Pepani aMalawi, a Chakwera anakutaitsani nthawi – Chaponda

Pepani aMalawi, a Chakwera anakutaitsani nthawi – Chaponda

A George Chaponda mtsogoleri wa mbali yotsutsa boma mnyumba ya malamulo, ati akupepesa onse amene anabwera lachisanu kudzamvera State of the Nation Address (SONA) yomwe a mtsogoleri wa dziko Lazarus Chakwera anapeleka.


A Chaponda ati anthuwo akanatha kutenga nthawi yawo kupanga zinthu zaphindu ku madela awo kuposa kumvera za ndale zomwe a Lazarus Chakwera amanena mnyumba ya malamulo.


A Chaponda afotokoza izi mnyumba ya malamulo lero pomwe aphungu akukumana kuyamba kulankhulapo pa zomwe mtsogoleri wa dziko anafotokoza zam’mene dziko lilili- SONA


A Chaponda ati mtsogoleri wa dziko waphonya mwayi ofotokozera za mavuto amene dziko lino likudutsamo ndipo ati, aMalawi a mchigawo chapakati atafunsidwa kuti moyo ulibwanji, kodi angakhonze kuvomeleza kuti zinthu zili bwino?.


Iwo ati aMalawi ndi omwe angaweluze za komwe dziko likupita.